LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb18 June tsa. 2
  • Tsatilani Mapazi a Khristu Mosamala Kwambili

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Tsatilani Mapazi a Khristu Mosamala Kwambili
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Nkhani Zofanana
  • Kondwelani Pamene Mukuzunzidwa
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • “Mulole Kuti Kupilila Kumalize Kugwila Nchito Yake”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2016
  • Mukhoza Kupilila Pamene Mukuzunzidwa
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Mmene Yehova Amatithandizira Kupirira
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
mwb18 June tsa. 2

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Tsatilani Mapazi a Khristu Mosamala Kwambili

Yesu anapeleka citsanzo cimene tiyenela kutengela, maka-maka ngati tikuyesedwa kapena kuzunzidwa. (1 Pet. 2:21-23) Olo kuti Yesu ananyozedwa na kuvutitsidwa, iye sanabwezele. (Maliko 15:29-32) N’ciani cinamuthandiza kupilila? Anali wofunitsitsa kucita cifunilo ca Yehova. (Yoh. 6:38) Cina, anasumika maganizo ake pa “cimwemwe cimene [Mulungu] anamuikila patsogolo pake.”—Aheb. 12:2.

Kodi timacita ciani ngati tivutitsidwa cifukwa ca cikhulupililo cathu? Akhristu oona ‘sabwezela coipa pa coipa.’ (Aroma 12:14, 17) Ngati titengela citsanzo ca Khristu ca kupilila, tidzakhala acimwemwe podziŵa kuti Mulungu akutiyanja.—Mat. 5:10-12; 1 Pet. 4:12-14.

TAMBANI VIDIYO YAKUTI DZINA LA YEHOVA N’LOFUNIKA KWAMBILI, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • Pamene Mlongo Pötzingera anali m’ndende ya yekha, kodi anaiseŵenzetsa bwanji nthawi mwanzelu?

  • Ni mavuto anji amene M’bale na Mlongo Pötzinger anapilila pamene anali m’ndende za cibalo?

  • N’ciani cinawathandiza kupilila?

Azimayi akugwila nchito ya kalavulagaga m’ndende, mu ulamulilo wa Nazi; M’bale na Mlongo Pötzinger

Mukamavutika, muzitsatila mapazi a Khristu mosamala kwambili

a Dzinali amailembanso kuti Poetzinger.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani