LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb18 August tsa. 8
  • Kunola Luso Lathu Mu Ulaliki—Kuseŵenzetsa Webusaiti Yathu ya JW.ORG

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kunola Luso Lathu Mu Ulaliki—Kuseŵenzetsa Webusaiti Yathu ya JW.ORG
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Nkhani Zofanana
  • Pezani Nzelu Zothandiza pa Umoyo pa JW.ORG
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Tingapeze Kuti Mayankho a Mafunso Ofunika Kwambili Onena za Umoyo?
    Tingapeze Kuti Mayankho a Mafunso Ofunika Kwambili Onena za Umoyo?
  • Mfundo Yothandiza Pa Kuŵelenga Kwanu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
  • Kodi Munadzifunsapo?
    Galamuka!—2019
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
mwb18 August tsa. 8
M’bale akuseŵenzetsa kakhadi kongenela pa webusaiti polongoza munthu webusaiti yathu ya jw.org

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Kunola Luso Lathu Mu Ulaliki—Kuseŵenzetsa Webusaiti Yathu ya JW.ORG

CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Cofalitsa ciliconse cophunzitsila Baibo ca mu Thuboksi yathu, cimatsogolela anthu ku webusaiti yathu ya jw.org. Ndipo tumakhadi tongenela pa webusaiti komanso kapepa kakuti Tingapeze Kuti Mayankho a Mafunso Ofunika Kwambili Onena za Umoyo? colinga cake cacikulu ni kutsogolela anthu ku webusaiti yathu. Mungaseŵenzetse webusaiti ya jw.org pogaŵila cofalitsa cophunzitsila Baibo ca mu Thuboksi yathu. Mungacite zimenezi mwa kutumizila munthu cofalitsaco pa imelo kapena mwa kumutumizila linki. Kucita izi kungakhale kothandiza kwambili maka-maka polalikila munthu amene amakamba citundu cina. Kuwonjezela apo, anthu angatifunse mafunso amene mayankho ake sapezeka m’zofalitsa za mu Thuboksi yathu. Zikakhala conco, tingaseŵenzetse webusaiti yathu, ndipo ulaliki wathu ungakhale wogwila mtima.

MMENE TINGACITILE:

  • Munthu akuseŵenzetsa kakhadi kongenela pa webusaiti kuti apite pa jw.org

    Seŵenzetsani mbali yakuti “ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA” (imene ipezeka ku Chichewa). Ngati mukulalikila kholo, ndipo lifuna kudziŵa zambili zokhudza kulela ana, mungapite pa ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA > ANTHU OKWATIRANA KOMANSO MABANJA.

  • Seŵenzetsani mbali yakuti “MABUKU.” Ngati mukucita ulaliki wamwayi ku sukulu, ndipo mufuna kugaŵila mnzanu wa m’kalasi kabuku kakuti Mayankho pa Mafunso 10 Amene Acicepele Amafunsa, mungapite pa MABUKU > MABUKU NDI TUMABUKU.

  • Seŵenzetsani mbali yakuti “ZOKHUDZA IFE.” Ngati mukulalikila mnzanu wa ku nchito amene afuna kuŵelengako zimene ise timakhulupilila, mungapite pa ZOKHUDZA IFE > MAFUNSO OFUNSIDWA KAŴILIKAŴILI OKHUDZA MBONI ZA YEHOVA.

TAMBANI VIDIYO YAKUTI KUSEŴENZETSA WEBUSAITI YATHU YA JW.ORG, NDIYENO GANIZILANI KUMENE MUNGAPITE PA WEBUSAITI YATHU KUTI MUTHANDIZE:

  • munthu amene sakhulupilila kuti kuli Mulungu

  • munthu amene wakumana na tsoka

  • m’bale kapena mlongo wozilala

  • munthu amene munamulalikila, ndipo afuna kudziŵa mmene timapezela ndalama zoyendetsela nchito yathu

  • munthu wa ku dziko lina amene afuna kukapezeka pa misonkhano m’dziko lawo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani