LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp21 na. 3 tsa. 15
  • Mungasankhe Mmene Tsogolo Lanu Lidzakhalile

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mungasankhe Mmene Tsogolo Lanu Lidzakhalile
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2021
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • KODI TINGACITE CIANI KUTI TIZIKONDA YEHOVA NA KUMVELA MAWU AKE?
  • Tsogolo Lanu Limadalila pa Zosankha Zanu!
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2018
  • Mungakhale pa Ubwenzi na Mulungu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2019
  • “Anthu Ofatsa Adzalandila Dziko Lapansi”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2018
  • Mawu Oyamba
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2021
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2021
wp21 na. 3 tsa. 15
Munthu ali pa malo odyela, ndipo akuonetsa mnzake zinazake pa foni.

Mungasankhe Mmene Tsogolo Lanu Lidzakhalile

Zaka pafupifupi 3,500 zapitazo, Yehova Mulungu anauza olambila ake zimene anayenela kucita kuti akhale na tsogolo labwino. Iye anati: “Ndaika moyo ndi imfa, dalitso ndi tembelelo pamaso panu. . . Conco inuyo ndi mbadwa zanu musankhe moyo kuti mukhalebe ndi moyo.”—Deuteronomo 30:19.

Kuti anthuwo akhale na tsogolo labwino, anafunika kusankha mwanzelu. N’zimenenso ife tiyenela kucita masiku ano. Baibo imatiuza mmene tingasankhile tsogolo labwino. Imati tiyenela ‘kukonda Yehova Mulungu wathu na kumvela mawu ake.’—Deuteronomo 30:20.

KODI TINGACITE CIANI KUTI TIZIKONDA YEHOVA NA KUMVELA MAWU AKE?

PHUNZILANI BAIBO: Kuti muzikonda Yehova, coyamba muyenela kuphunzila za iye m’Baibo. Pamene muphunzila, mudzaona kuti iye ni Mulungu wacikondi amene amakufunilani zabwino. Amakupemphani kuti muzipemphela kwa iye “cifukwa amakudelani nkhawa.” (1 Petulo 5:7) Baibo imati ngati muyesetsa kuyandikila Mulungu, “iyenso adzakuyandikilani.”—Yakobo 4:8.

MUZISEŴENZETSA ZIMENE MUMAPHUNZILA: Kumvela Mulungu kumatanthauza kumvela malangizo ake anzelu opezeka m’Baibo. Mukatelo, ‘mudzakhala ndi moyo wopambana, ndipo mudzacita zinthu mwanzelu.’—Yoswa 1:8.

Kuti muphunzile zambili, pitani pa webusaiti yathu ya jw.org. Pamenepo mungaŵelenge Baibo, kucita maphunzilo a Baibo a pa Intaneti,a kapena kupempha munthu woti azikuphunzitsani Baibo kuti muimvetsetse.

Sankhani kuphunzila Baibo palipano kuti ikuthandizeni kukhala na tsogolo labwino!

a Maphunzilowa amapezeka m’zinenelo 7, kuphatikizapo ci Chinese Mandarin, ci Chinese Cantonese, komanso Cizungu.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani