LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w23 August tsa. 32
  • Mfundo Yothandiza Pa Kuŵelenga Kwanu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mfundo Yothandiza Pa Kuŵelenga Kwanu
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • Pezani Cuma ca Kuuzimu Cokhudza Yehova
  • Pezani Cuma Cauzimu Comwe Mungaseŵenzetse
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
  • Kodi Yehova ni Mulungu Wotani?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Cida Catsopano Cofufuzila
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Pitilizani Kuvala “Umunthu Watsopano” Pambuyo pa Ubatizo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
w23 August tsa. 32

Mfundo Yothandiza Pa Kuŵelenga Kwanu

Pezani Cuma ca Kuuzimu Cokhudza Yehova

Tikamaŵelenga Baibo, tingagwilitse nchito zida zosiyana-siyana kuti timvetsetse zimene tikuŵelengazo. Colinga cathu poŵelenga sikungowonjezela cidziŵitso ca m’Baibo ayi. Koma timafuna kupeza cuma cauzimu cokhudza makhalidwe a Yehova, kuti tikulitse cikondi cathu pa iye. Kuti ticite zimenezi, tizidzifunsa kuti, ‘Kodi nkhaniyi iniphunzitsa ciyani za Yehova?’

Mungafufuze umboni woonetsa mmene Yehova wakhala akuonetsela cikondi, nzelu, cilungamo, na mphamvu. Koma Yehova alinso na makhalidwe ena ambili osililika. N’kuti kumene tingapeze mfundo zambili zokhudza makhalidwe ake?

Onani m’ndandanda wa makhalidwe a Yehova oposa 50 m’buku la cizungu la kuti Watch Tower Publications Index. Pitani pa mutu wakuti “Jehovah.” Ndiyeno pitani kamutu kakuti “Qualities by Name.” Fufuzani makhalidwe amene agwilizana na nkhani ya m’Baibo imene mukuŵelengayo. (Ngati mulibe bukuli, gwilitsani nchito Buku Lofufuzila Nkhani la Mboni za Yehova. Pitani pa mutu wakuti “Yehova Mulungu.” Kenaka pitani pa kamutu kakuti “Makhalidwe a Yehova.”)

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani