LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp25 na. 1 tsa. 9
  • Cifukwa Cake Nkhondo Zikupitilizabe Kucitika

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Cifukwa Cake Nkhondo Zikupitilizabe Kucitika
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • CHIMO
  • MABOMA A ANTHU
  • SATANA NDI ZIWANDA ZAKE
  • Kodi Nkhondo Zidzatha Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
  • Kodi Cifunilo ca Mulungu Kwa Anthu N’ciani?
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Mmene Nkhondo Zimatikhudzila Tonsefe
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
  • Kodi Ndani Maka-maka Amacititsa Nkhondo ndi Mavuto?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
wp25 na. 1 tsa. 9

Cifukwa Cake Nkhondo Zikupitilizabe Kucitika

Baibo imafotokoza zimene zimayambitsa nkhondo, komanso cifukwa cake nkhondo zikupitilizabe kucitika.

CHIMO

Mulungu analenga makolo athu oyambilila, Adamu ndi Hava, m’cifanizilo cake. (Genesis 1:27) Izi zitanthauza kuti iwo anali kutha kuonetsa makhalidwe amene Mulungu ali nawo, monga mtendele ndi cikondi. (1 Akorinto 14:33; 1 Yohane 4:8) Koma Adamu ndi Hava sanamvele Mulungu ndipo anacimwa. Zotsatilapo zake n’zakuti tonsefe tinatengela ucimo ndi imfa kwa iwo. (Aroma 5:12) Ucimo umenewo umatipangitsa kukhala ndi maganizo oipa. Ici n’cifukwa cake anthu ambili amacita zaciwawa.​—Genesis 6:5; Maliko 7:​21, 22.

MABOMA A ANTHU

Mulungu sanatilenge kuti tizidzilamulila tokha. Baibo imati: “Munthu amene akuyenda alibe ulamulilo wowongolela mapazi ake.” (Yeremiya 10:23) Pa cifukwa cimeneci, maboma a anthu sangakwanitse kuthetsa nkhondo ndi zaciwawa.

SATANA NDI ZIWANDA ZAKE

Baibo imaonetsa kuti “dziko lonse lili m’manja mwa woipayo.” (1 Yohane 5:19) “Woipayo” ndi Satana Mdyelekezi, ndipo iye ndi wopha anthu. (Yohane 8:44) Iye ndi ziwanda zake amalimbikitsa anthu kuti azicita nkhondo ndi ciwawa.​—Chivumbulutso 12:​9, 12.

Anthu sangakwanitse kuthetsa zinthu zimene zimayambitsa nkhondo ndi ciwawa. Koma Mulungu yekha ndiye angathe kucita zimenezi.

Zipembedzo pa Nkhondo

Nthawi zambili zipembedzo zimalekelela, kuvomeleza kapena kulimbikitsa nkhondo. Zipembedzo zimene zimacita zimenezi ndi zabodza, ndipo Baibo imazicha “Babulo Wamkulu.” (Chivumbulutso 18:2) Mulungu amati Babulo Wamkulu ndiye anacititsa imfa “za anthu onse amene anaphedwa padziko lapansi.” (Chivumbulutso 18:24) Kuti mudziwe zambili, welengani nkhani yakuti “Kodi Babulo Wamkulu N’ciyani?” pa jw.org ku Chichewa.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani