LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mrt nkhani 109
  • Yesu Adzacotsapo Anthu Osamvela Malamulo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Yesu Adzacotsapo Anthu Osamvela Malamulo
  • Nkhani Zina
  • Nkhani Zofanana
  • Yesu Adzathetsa Umphawi
    Nkhani Zina
  • Yesu Adzathetsa Nkhondo
    Nkhani Zina
  • Ndani Amene Mungadalile?—Kodi Baibulo Ikutipo Ciyani?
    Nkhani Zina
  • Kuwonjezeka kwa Kusamvela Malamulo Padziko Lonse—Kodi Baibo Ikutipo Ciyani?
    Nkhani Zina
Onaninso Zina
Nkhani Zina
mrt nkhani 109
Cigaŵenga cikuŵendelela mzimayi amene ali yekha. Mzimayiyo waciona ndipo akutuma foni popempha thandizo.

alfa27/stock.adobe.com

Yesu Adzacotsapo Anthu Osamvela Malamulo

Yesu adziŵa mmene cimamvekela munthu akamavutika cifukwa ca kusamvela malamulo na kupanda cilungamo kwa anthu ena. Iye anaimbidwapo mlandu wabodza, kumenyedwa, kuweluzidwa mopanda cilungamo, komanso kufa imfa yowawa. Ngakhale kuti anali wosalakwa, iye anali wokonzeka kupeleka “moyo wake dipo kuti awombole anthu ambili.” (Mateyu 20:28; Yohane 15:13) Tsopano pokhala Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, iye adzabweletsa cilungamo padziko lonse lapansi, ndipo adzathetselatu zopanda cilungamo zonse.—Yesaya 42:3.

Baibo imafotokoza mmene dziko lapansi lidzakhalila Yesu akadzacitapo kanthu. Imati:

  • “Oipa sadzakhalaponso. Udzayangʼana pamene ankakhala, ndipo sadzapezekapo. Koma anthu ofatsa adzalandila dziko lapansi, ndipo adzasangalala ndi mtendele woculuka.”—Salimo 37:10, 11.

Kodi tingaonetse bwanji kuti timayamikila zimene Yesu anaticitila komanso zimene adzaticitila m’tsogolo? Njila imodzi ndi mwakuphunzila zambili zokhuza “uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu” umene Yesu anali kulalikila. (Luka 4:43) Welengani nkhani yakuti “Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?”

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani