LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Lelo

Ciŵili, November 4

Iwe Imfa amene umabweletsa ululu woopsa, kodi mphamvu yako ili kuti?​—Hos. 13:14.

Kodi Yehova alidi na cifuno coukitsa akufa? Indedi. Iye anauzila olemba Baibo ambili kulemba lonjezo lake lakuti kutsogoloku adzaukitsa akufa. (Yes. 26:19; Chiv. 20:11-13) Ndipo Yehova akalonjeza, nthawi zonse amakwanilitsa lonjezo lake. (Yos. 23:14) Yehova ni wofunitsitsa kuukitsa akufa. Ganizilani mawu a Yobu. Iye anali wotsimikiza kuti ngakhale atafa, Yehova adzalakalaka kumuonanso. (Yobu 14:14, 15) Yehova amalakalakanso kuukitsa alambili ake onse amene anamwalila. Amafunitsitsa kudzawaukitsa kuti akakhale na moyo wathanzi komanso wacimwemwe. Nanga bwanji za mabiliyoni amene anamwalila asanakhale na mwayi wophunzila coonadi cokhudza Yehova? Mulungu wathu wacikondi amafuna kuwaukitsa nawonso. (Mac. 24:15) Amafuna kuti akawapatse mwayi wokhala mabwenzi ake, komanso kuti akakhale na moyo kwamuyaya padziko lapansi.​—Yoh. 3:16. w23.04 9 ¶5-6

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Citatu, November 5

Mulungu adzatipatsa mphamvu.​—Sal. 108:13.

Kodi mungalimbikitse bwanji ciyembekezo canu? Mwacitsanzo, ngati muli na ciyembekezo codzakhala na moyo kwamuyaya padziko lapansi, muziŵelenga Malemba amene amafotokoza mmene Paradaiso adzakhalile na kuwasinkhasinkha. (Yes. 25:8; 32:16-18) Muziganizila mmene umoyo udzakhalile m’dziko latsopano. Yelekezelani kuti muli m’dzikolo. Tikamaganizila kwambili za ciyembekezo cathu ca dziko latsopano tidzaona mavuto athu kuti ni “akanthawi ndipo ndi opepuka.” (2 Akor. 4:17) Yehova adzakupatsani mphamvu kupitila mu ciyembekezo cimene wakupatsani. Wapeleka zonse zofunika kuti mulandile mphamvu zocokela kwa iye. Conco, mukafuna thandizo kuti mucite utumiki wina wake, kupilila mayeso, kapena kukhalabe na cimwemwe, mufikileni Yehova m’pemphelo mocokela pansi pa mtima, na kufuna-funa citsogozo cake mwa kucita phunzilo la munthu mwini. Cina landilani cilimbikitso kucokela kwa Akhristu anzanu. Komanso sungani ciyembekezo canu cili cowala. Citani zimenezi kuti “mulandile mphamvu zazikulu mogwilizana ndi mphamvu zake zocititsa mantha, nʼcolinga coti muthe kupilila zinthu zonse moleza mtima ndiponso mwacimwemwe.”​—Akol. 1:11. w23.10 17 ¶19-20

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Cinayi, November 6

Muzithokoza pa ciliconse.​—1 Ates. 5:18.

Tili na zifukwa zambili zoyamikila Yehova m’pemphelo. Tingamuyamikile pa zabwino zonse zimene tili nazo, cifukwa mphatso iliyonse yabwino imacokela kwa iye. (Yak. 1:17) Tingamuyamikile cifukwa cotipatsa dziko lapansi lokongola, na zinthu zacilengedwe zocititsa cidwi. Tingamuyamikilenso potipatsa moyo, banja, mabwenzi, komanso ciyembekezo. Ndipo tingamuyamikilenso potilola kukhala naye pa ubwenzi wamtengo wapatali. Aliyense pacake angafunike kuyesetsa kuti apeze zifukwa zomuyamikila Yehova. Anthu ambili m’dzikoli ni osayamika. Amaika maganizo awo pa zimene akufuna, m’malo moyamikila zimene ali nazo kale. Ngati mzimu umenewu ungatiyambukile, mapemphelo athu angamakhale mndandanda wa zopempha basi. Kuti tipewe zimenezi, tiyenela kupitiliza kukulitsa mzimu woyamikila pa zonse zimene Yehova amaticitila.​—Luka 6:45. w23.05 4 ¶8-9

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani