LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Lelo

Mande, September 1

Kuwala kwa m’mawa kudzatifikila kucokela kumwamba.​—Luka 1:78.

Mulungu anapatsa Yesu mphamvu zocotsapo mavuto onse a anthu. Mwa zozizwitsa zake, Yesu anaonetsa kuti ali na mphamvu zocotsapo mavuto onse omwe pa ife tokha sitingathe kuwacotsapo. Mwacitsanzo, iye ali na mphamvu zotimasula ku zonse zotibweletsela mavuto​—ucimo, matenda, na imfa. (Mat. 9:1-6; Aroma 5:12, 18, 19) Zozizwitsa zake zinaonetsa kuti angathe kucilitsa “matenda amtundu uliwonse,” ngakhale kuukitsa akufa. (Mat. 4:23; Yoh. 11:43, 44) Cina, ali na mphamvu zolamulila mphepo zoopsa komanso kumasula anthu ku mizimu yoipa. (Maliko 4:37-39; Luka 8:2) N’zolimbikitsa zedi kudziŵa kuti Yehova anapatsa Mwana wake mphamvu zimenezi! Tingakhale na cidalilo conse kuti Ufumu wa Mulungu udzabweletsadi madalitso kutsogoloku. Zozizwitsa zimene Yesu anacita monga munthu padziko lapansi, zitiphunzitsa kuti kutsogoloku adzacita zambili monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu. w23.04 3 ¶5-7

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Ciŵili, September 2

Mzimu umafufuza zinthu zonse, ngakhale zinthu zozama za Mulungu.​—1 Akor. 2:10.

Ngati muli mumpingo waukulu ndipo nthawi zambili mumaona kuti simupatsidwa mwayi wopelekapo ndemanga, mungaganize zongoleka kupelekapo ndemanga. Koma conde musaleke. Muzikonzekela ndemanga zingapo pa msonkhano uliwonse. Ngati sanakupatseni mwayi wopeleka ndemanga kumayambililo kwa msonkhano, mudzakhalabe na mipata ina yopelekapo ndemanga pamene msonkhanowo ukupitiliza. Mukamakonzekela Nsanja ya Mlonda, muziganizila mmene ndime iliyonse ikugwilizanila na mfundo yaikulu ya nkhaniyo. Mukatelo, mudzakhala na ndemanga zabwino zimene mungapeleke pa phunzilo lonselo. Kuwonjezela apo, mungakonzekele kukapeleka ndemanga pa ndime zokamba pa ziphunzitso zozama za m’Baibo zovuta kuzifotokoza. Cifukwa ciyani? Cifukwa ni anthu ocepa angakweze manja kuti apeleke ndemanga. Nanga bwanji ngati pambuyo pa misonkhano ingapo sanakupatsenibe mwayi wopeleka ndemanga? Msonkhano usanayambe, uzani wotsogoza ndime imene mwakonzekela kupeleka ndemanga. w23.04 21-22 ¶9-10

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Citatu, September 3

Yosefe . . . [anacita] mogwilizana ndi zimene mngelo wa Yehova anamuuza. Anatenga mkazi wake nʼkupita naye kunyumba.​—Mat. 1:24.

Mofunitsitsa Yosefe anatsatila citsogozo ca Yehova. Mwa ici, anakhala mwamuna wabwino. Katatu konse, Mulungu anam’patsa malangizo okhudza banja lake. Pa nthawi zonsezo, anatsatila malangizowo ngakhale pamene zinali zovuta kutelo. (Mat. 1:20; 2:13-15, 19-21) Cifukwa cotsatila malangizo a Mulungu, Yosefe anateteza Mariya, kum’thandiza, komanso kum’samalila. Izi zinapangitsa Mariya kuti azim’konda Yosefe na kum’lemekeza. Inu amuna, mungatengele citsanzo ca Yosefe mwa kutsatila ulangizi wa m’Baibo posamalila banja lanu. Mukatelo, ngakhale pamene n’zovuta, mumaonetsa kuti mumam’konda mkazi wanu, ndipo mumalimbitsa ukwati wanu. Mlongo wina ku Vanuatu, amene wakhala m’banja zaka zoposa 20 anati: “Mwamuna wanga akamafufuza na kutsatila malangizo a m’Baibo, nimam’lemekeza kwambili. Nimamva kukhala wotetezeka, ndipo sinimakayikila zisankho zake.” w23.05 21 ¶5

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani