Ciŵili, September 2
Mzimu umafufuza zinthu zonse, ngakhale zinthu zozama za Mulungu.—1 Akor. 2:10.
Ngati muli mumpingo waukulu ndipo nthawi zambili mumaona kuti simupatsidwa mwayi wopelekapo ndemanga, mungaganize zongoleka kupelekapo ndemanga. Koma conde musaleke. Muzikonzekela ndemanga zingapo pa msonkhano uliwonse. Ngati sanakupatseni mwayi wopeleka ndemanga kumayambililo kwa msonkhano, mudzakhalabe na mipata ina yopelekapo ndemanga pamene msonkhanowo ukupitiliza. Mukamakonzekela Nsanja ya Mlonda, muziganizila mmene ndime iliyonse ikugwilizanila na mfundo yaikulu ya nkhaniyo. Mukatelo, mudzakhala na ndemanga zabwino zimene mungapeleke pa phunzilo lonselo. Kuwonjezela apo, mungakonzekele kukapeleka ndemanga pa ndime zokamba pa ziphunzitso zozama za m’Baibo zovuta kuzifotokoza. Cifukwa ciyani? Cifukwa ni anthu ocepa angakweze manja kuti apeleke ndemanga. Nanga bwanji ngati pambuyo pa misonkhano ingapo sanakupatsenibe mwayi wopeleka ndemanga? Msonkhano usanayambe, uzani wotsogoza ndime imene mwakonzekela kupeleka ndemanga. w23.04 21-22 ¶9-10
Citatu, September 3
Yosefe . . . [anacita] mogwilizana ndi zimene mngelo wa Yehova anamuuza. Anatenga mkazi wake nʼkupita naye kunyumba.—Mat. 1:24.
Mofunitsitsa Yosefe anatsatila citsogozo ca Yehova. Mwa ici, anakhala mwamuna wabwino. Katatu konse, Mulungu anam’patsa malangizo okhudza banja lake. Pa nthawi zonsezo, anatsatila malangizowo ngakhale pamene zinali zovuta kutelo. (Mat. 1:20; 2:13-15, 19-21) Cifukwa cotsatila malangizo a Mulungu, Yosefe anateteza Mariya, kum’thandiza, komanso kum’samalila. Izi zinapangitsa Mariya kuti azim’konda Yosefe na kum’lemekeza. Inu amuna, mungatengele citsanzo ca Yosefe mwa kutsatila ulangizi wa m’Baibo posamalila banja lanu. Mukatelo, ngakhale pamene n’zovuta, mumaonetsa kuti mumam’konda mkazi wanu, ndipo mumalimbitsa ukwati wanu. Mlongo wina ku Vanuatu, amene wakhala m’banja zaka zoposa 20 anati: “Mwamuna wanga akamafufuza na kutsatila malangizo a m’Baibo, nimam’lemekeza kwambili. Nimamva kukhala wotetezeka, ndipo sinimakayikila zisankho zake.” w23.05 21 ¶5
Cinayi, September 4
Kumeneko kudzakhala msewu waukulu inde msewu umene udzachedwa Msewu Wopatulika.—Yes. 35:8.
Ayuda obwelela kwawo anali kudzakhala “anthu oyela” kwa Mulungu wawo. (Deut. 7:6) Komabe, izi sizinatanthauze kuti sanafunike kupanga masinthidwe kuti Yehova awayanje. Ayuda ambili anabadwila ku Babulo, ndipo n’kutheka kuti anatengela maganizo na cikhalidwe ca Ababulo. Patapita zaka zambili Ayuda oyamba atabwelela ku Isiraeli, Bwanamkubwa Nehemiya anadabwa ataona kuti ana obadwila ku Isiraeli sanali kudziŵa cinenelo ca Ayuda. (Deut. 6:6, 7; Neh. 13:23, 24) Popeza mbali yaikulu ya Mawu a Mulungu inali m’Ciheberi, kodi anawo akanaphunzila bwanji kukonda Yehova na kum’lambila? (Ezara 10:3, 44) Conco, Ayudawo anafunika kupanga masinthidwe aakulu. Koma cikanakhala copepuka kwa iwo kucita zimenezo ku Isiraeli komwe kulambila koona kunali kubwezeletsedwa mwapang’ono-pang’ono.—Neh. 8:8, 9. w23.05 15 ¶6-7