LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb19 October tsa. 7
  • Kodi Mumawakonda Kwambili Mawu a Mulungu?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Mumawakonda Kwambili Mawu a Mulungu?
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Nkhani Zofanana
  • Thandizo Ilipo
    Galamuka!—2020
  • Colinga ca Webu Saiti Yathu Ndi Kuthandiza Ife ndi Anthu Ena
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Pezani Nzelu Zothandiza pa Umoyo pa JW.ORG
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • 12 Zolinga
    Galamuka!—2018
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
mwb19 October tsa. 7

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Kodi Mumawakonda Kwambili Mawu a Mulungu?

M’Baibo muli mawu na maganizo a Yehova Mulungu, Mlembi wa buku lopatulika limeneli. (2 Pet. 1:20, 21) Mwa kugogomeza nkhani ya kukweza ulamulilo wa Mulungu kupitila mu Ufumu wake, Baibo imapatsa anthu ciyembekezo cakuti posacedwa, umoyo udzakhala wabwino. Baibo imaonetsanso umunthu wacikondi wa Atate wathu, Yehova.—Sal. 86:15.

Tonsefe timalemekeza Mawu a Yehova pa zifukwa zosiyana-siyana. Koma kodi timaonetsa kuti timakonda mphatso ya mtengo wapatali imeneyi mwa kuiŵelenga nthawi zonse, na kuseŵenzetsa mfundo zake mu umoyo wathu? Tiyeni tizionetsa mwa zocita zathu kuti tili na maganizo ofanana na a wamasalimo amene anati: “Ndimakonda kwambili cilamulo canu!—Sal. 119:97.

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI, ANAILEMEKEZA KWAMBILI BAIBO—KAMBALI KAKE (WILLIAM TYNDALE), NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • William Tyndale; William Tyndale pa makina opulintila; kope yoyamba ya Baibo ya Cipangano Catsopano imene Tyndale anamasulila

    N’cifukwa ciani William Tyndale anamasulila mbali zina za Baibo?

  • N’cifukwa ciani khama lake pomasulila Baibo linali locititsa cidwi?

  • Kodi makope a Baibo imene Tyndale anamasulila anali kuwazembetsa bwanji kuloŵa m’dziko la England?

  • Kodi aliyense wa ife angaonetse bwanji kuti amakonda Mawu a Mulungu

ZOFUNIKA KUSINKHA-SINKHA: Kodi Mawu a Mulungu afanana bwanji na . . .

  • nyale komanso kuwala? —Sal. 119:105)

  • madzi?— Aef. 5:26)

  • lupanga?—Aef. 6:17)

  • galasi?—Yak. 1:23-25)

MUZIŴELENGA MAWU A MULUNGU TSIKU LILILONSE

Ndandanda Yoŵelengela Baibo

Kodi munayesako kuseŵenzetsa Ndandanda Yowerengera Baibulo imene ili pa jw.org m’chichewa? Ndandanda ya mpangidwe wa PDF, imakupelekani pa jw.org komanso pa Lemba limene mufuna kuŵelenga. Ngati Baibo yongomvetsela ilimo m’citundu canu, nayonso mungaipeze pa jw.org.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani