LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb23 September tsa. 5
  • Muzidalila Yehova Pamene Mukuvutitsidwa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Muzidalila Yehova Pamene Mukuvutitsidwa
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Nkhani Zofanana
  • Ningacite Bwanji Ngati Ena Amanivutitsa Kusukulu?
    Mayankho pa Mafunso 10 Amene Acicepele Amafunsa
  • Zisankho Zimene Zimaonetsa Kuti Timadalila Yehova
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Makolo—Phunzitsani Ana Anu Kukondweletsa Mulungu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Sitinakhalepo Tokha Ngakhale Pang’ono
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
mwb23 September tsa. 5
Mtsikana akuonetsa makolo foni yake, ndipo akuwafotokozela mmene akumvela. Makolo ake akumvetsela mwachelu.

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Muzidalila Yehova Pamene Mukuvutitsidwa

Anthu ovutitsa anzawo angacite zinthu zimene zingativulaze, komanso kutipweteka mtima. Angacititsenso kuti ubwenzi wathu na Yehova uwonongeke ngati ticita mantha pamene akutsutsa kulambila kwathu. Kodi mungadziteteze bwanji kwa anthu ovutitsa anzawo?

Alambili a Yehova ambili, akwanitsa kuthana na ovutitsa anzawo mwa kudalila Yehova. (Sal. 18:17) Mwacitsanzo, Esitere molimba mtima anaulula ciwembu ca munthu wankhanza dzina lake Hamani. (Esitere 7:​1-6) Asanacite zimenezo, iye anaonetsa kudalila Yehova mwa kusala kudya. (Esitere 4:​14-16) Yehova anam’dalitsa Esitere pa zimene anacita mwa kumuteteza pamodzi na anthu ake.

Inu acicepele, ngati mumavutitsidwa, pemphani Yehova kuti akuthandizeni. Komanso uzan’koni munthu wina wacikulile monga makolo anu za vuto lanulo. Khalani wotsimikiza kuti nanunso Yehova adzakuthandizani mmene anathandizila Esitere. N’ciyani cina cingakuthandizeni ngati mumavutitsidwa?

ONELELANI VIDIYO YAKUTI UMOYO WANGA NILI WACICEPELE—KODI KUVUTITSIDWA MUNGATHANE NAKO BWANJI? KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

  • Kodi acinyamata angaphunzilepo ciyani pa citsanzo ca Charlie na Ferin?

  • Kodi makolo angaphunzilepo ciyani pa zimene Charlie na Ferin anakamba pankhani yothandiza ana kuthana na munthu wowavutitsa?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani