Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Salimo 53:kam-6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimboyi iimbidwe potsatira kaimbidwe ka Mahalati.* Masikili.* Salimo la Davide.

      53 Munthu wopusa* amanena mumtima mwake kuti:

      “Kulibe Yehova.”+

      Zochita zopanda chilungamo za anthu amenewa ndi zoipa komanso zonyansa,

      Ndipo palibe amene akuchita zabwino.+

       2 Koma kuchokera kumwamba, Mulungu amayangʼana ana a anthu,+

      Kuti aone ngati pali aliyense wozindikira, ngati pali aliyense amene akufunafuna Yehova.+

       3 Onse apatuka,

      Ndipo onsewo ndi achinyengo.

      Palibe aliyense amene akuchita zabwino,

      Palibiretu ndi mmodzi yemwe.+

       4 Kodi palibe aliyense womvetsa zinthu pakati pa anthu ochita zoipawa?

      Iwo amadya anthu anga ngati kuti akudya chakudya.

      Ndipo sapemphera kwa Yehova.+

       5 Koma adzagwidwa ndi mantha aakulu,

      Mantha amene sanayambe agwidwapo chiyambire,*

      Chifukwa Mulungu adzamwaza mafupa a anthu amene akukuukirani.*

      Mudzawachititsa manyazi chifukwa Yehova wawakana.

       6 Zikanakhala bwino chipulumutso cha Isiraeli chikanachokera ku Ziyoni.+

      Yehova akadzabwezeretsa anthu ake amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina,

      Yakobo adzasangalale, Isiraeli adzakondwere.

  • Aroma 3:10-12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani