Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • mwb21.07 14
  • Muziwafika Pamtima

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muziwafika Pamtima
  • Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Nkhani Yofanana
  • Zimene Mungachite Kuti Muzisangalala Kwambiri Mu Utumiki​—Muzifunsa Mafunso
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Zimene Mungachite Kuti Muzisangalala Kwambiri mu Utumiki
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Muzilola Kuti Yehova Azikuthandizani Kudzera M’pemphero
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Muzithandiza Ophunzira Baibulo Kuti Asiye Makhalidwe Oipa
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
Onani Zambiri
Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
mwb21.07 14

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI | ZIMENE MUNGACHITE KUTI MUZISANGALALA KWAMBIRI MU UTUMIKI

Muziwafika Pamtima

Kumvera Mulungu kumayambira mumtima. (Miy 3:1) Choncho mukamaphunzitsa anthu Baibulo, muziyesetsa kuwafika pamtima. Kodi mungachite bwanji zimenezi?

Musamangophunzitsa ophunzira anu mfundo za choonadi cha m’Baibulo, koma muziwathandiza kuona mmene mfundozo zikukhudzira moyo wawo komanso ubwenzi wawo ndi Yehova. Muziwathandiza kumvetsa bwino mmene mfundo za m’Baibulo zimasonyezera chikondi, ubwino, komanso chilungamo cha Mulungu. Mosamala komanso mokoma mtima, muziwafunsa mafunso omwe angawathandize kuganizira mmene akumvera chifukwa cha zimene akuphunzirazo. Athandizeni kudziwa mmene kusintha mmene amaganizira kapena kusiya khalidwe linalake loipa kungawathandizire. Mukaona munthu amene mukuphunzira naye Baibulo akukonda Yehova ndi mtima wonse, mudzakhala wosangalala kwambiri.

ONERANI VIDIYO YAKUTI MUZIWONJEZERA LUSO LANU KUTI MUZISANGALALA NDI NTCHITO YOPHUNZITSA​—MUZIWAFIKA PAMTIMA, NDIPO KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti ‘Muziwonjezera Luso Lanu Kuti Muzisangalala ndi Ntchito Yophunzitsa​—Muziwafika Pamtima.’ Anita akufunsa Jane funso pa nthawi ya phunziro la Baibulo.

    N’chifukwa chiyani Anita anafunsa Jane kuti: “Unaganiziraponso zimene tinakambirana Monday?”

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti ‘Muziwonjezera Luso Lanu Kuti Muzisangalala ndi Ntchito Yophunzitsa​—Muziwafika Pamtima.’ Anita akufotokoza pogwiritsa ntchito malemba.

    Kodi Anita anathandiza bwanji Jane kumvetsa kuti mfundo za m’Baibulo zimasonyeza kuti Yehova amamukonda?

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti ‘Muziwonjezera Luso Lanu Kuti Muzisangalala ndi Ntchito Yophunzitsa​—Muziwafika Pamtima.’ Jane akumvetsera Anita.

    Tikamayesetsa kuwafika pamtima anthu omwe timaphunzira nawo, zidzawalimbikitsa kuti apite patsogolo

    Kodi Anita anathandiza bwanji Jane kuganizira mmene angasonyezere kuti amakonda Mulungu?

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani