NYIMBO 5
Ntchito Zodabwitsa za Mulungu
zosindikizidwa
1. M’lungu mumandidziwa bwino,
Ndikagona ndipo ndikadzuka.
Mumafufuza maganizo anga,
Mawu ndi njira zanganso
mumadziwa.
Munandiona ndili m’mimba,
Munaonanso mafupa anga.
Munalemba ziwalo zanga zonse.
M’lungu wamphamvu
ndidzakutamandani.
Nzeru zanu, Mulungu, n’zodabwitsa;
Zimenezi ndithu ndikudziwa.
Ndikaopa kupezedwa ndi mdima,
Mzimu wanu udzandipezabe.
N’kuti komwe ndingabisale,
Komwe inu simungandione?
Kumanda kodi kapena kumwamba
Mumdima, m’nyanja;
ayi ndithu kulibe.
(Onaninso Sal. 66:3; 94:19; Yer. 17:10.)