Levitiko 18:22 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 22 “‘Usagone ndi mwamuna+ mmene umagonera ndi mkazi.+ N’chonyansa chimenechi. Levitiko 20:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 “‘Mwamuna akagona ndi mwamuna mnzake, mmene mwamuna amagonera ndi mkazi, onse awiri achita chinthu chonyansa.+ Iwo aziphedwa ndithu. Mlandu wa magazi awo ukhale wa iwo eni. Aroma 1:27 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 27 Amunanso chimodzimodzi. Iwo anasiya njira yachibadwa yofuna akazi+ n’kumatenthetsana okhaokha mwachiwawa m’chilakolako choipa, amuna ndi amuna anzawo,+ kuchitirana zonyansa+ ndi kulandiriratu mphoto+ yoyenerera kulakwa kwawo.+ 1 Akorinto 6:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Kodi zoonadi inu simukudziwa kuti anthu osalungama sadzalowa mu ufumu wa Mulungu?+ Musasocheretsedwe. Adama,+ opembedza mafano,+ achigololo,+ amuna amene amagonedwa ndi amuna anzawo,+ amuna ogona amuna anzawo,+ Yuda 7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Komanso mizinda ya Sodomu ndi Gomora ndi mizinda yozungulira mizinda imeneyi,+ inalandira chilango cha moto wosatha,+ motero yaikidwa monga chitsanzo chotichenjeza.+ Anthu ake anachita mofanana ndi amene tatchula aja, pochita dama loipitsitsa ndiponso pogonana m’njira imene si yachibadwa.+
13 “‘Mwamuna akagona ndi mwamuna mnzake, mmene mwamuna amagonera ndi mkazi, onse awiri achita chinthu chonyansa.+ Iwo aziphedwa ndithu. Mlandu wa magazi awo ukhale wa iwo eni.
27 Amunanso chimodzimodzi. Iwo anasiya njira yachibadwa yofuna akazi+ n’kumatenthetsana okhaokha mwachiwawa m’chilakolako choipa, amuna ndi amuna anzawo,+ kuchitirana zonyansa+ ndi kulandiriratu mphoto+ yoyenerera kulakwa kwawo.+
9 Kodi zoonadi inu simukudziwa kuti anthu osalungama sadzalowa mu ufumu wa Mulungu?+ Musasocheretsedwe. Adama,+ opembedza mafano,+ achigololo,+ amuna amene amagonedwa ndi amuna anzawo,+ amuna ogona amuna anzawo,+
7 Komanso mizinda ya Sodomu ndi Gomora ndi mizinda yozungulira mizinda imeneyi,+ inalandira chilango cha moto wosatha,+ motero yaikidwa monga chitsanzo chotichenjeza.+ Anthu ake anachita mofanana ndi amene tatchula aja, pochita dama loipitsitsa ndiponso pogonana m’njira imene si yachibadwa.+