16 Unali kuchita malonda ndi Edomu chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako. Unapereka zinthu zimene unasunga posinthanitsa ndi miyala ya nofeki,+ ubweya wa nkhosa wonyika mu utoto wofiirira, nsalu zamitundu yosiyanasiyana, nsalu zabwino kwambiri, miyala yamtengo wapatali ya korali ndi ya rube.