24 Kenako Mose anaitana ana a Aroni ndi kuwapaka magazi m’munsi pakhutu lawo la kudzanja lamanja, pachala chawo chamanthu kudzanja lamanja ndi pachala chawo chachikulu cha kumwendo wa kudzanja lamanja. Koma Mose anawaza magazi otsalawo mozungulira paguwa lansembe.+