25 Kenako anapanga guwa lansembe zofukiza+ la matabwa a mthethe.+ M’litali mwake linali mkono umodzi, m’lifupi mwake mkono umodzi. Mbali zake zonse zinayi zinali zofanana, ndipo msinkhu wake unali mikono iwiri. Guwalo linali ndi nyanga pamwamba pake.+