20 Mwana woyamba kubadwa wa bulu muzimuwombola ndi nkhosa.+ Koma ngati simungamuwombole, muzimupha mwa kum’thyola khosi. Ndipo aliyense woyamba kubadwa mwa ana anu aamuna muzimuwombola.+ Palibe amene ayenera kuonekera kwa ine ali chimanjamanja.+
27 Koma nyama yodetsedwa+ yoyamba kubadwa angaiwombole. Ngati munthu akufuna kuiwombola azipereka mtengo wa nyamayo n’kuwonjezerapo limodzi mwa magawo asanu a mtengowo.+ Koma ngati mwiniwake wa nyamayo saiwombola wansembe aziigulitsa pa mtengo woikidwiratu.