13 Asa ndi anthu amene anali naye anawathamangitsa mpaka kukafika ku Gerari,+ ndipo Aitiyopiyawo anapitiriza kuphedwa mpaka palibe amene anatsala ndi moyo, popeza Yehova+ ndi gulu lake+ anawagonjetseratu. Pambuyo pake, anthuwo anatenga zofunkha zochuluka zedi.+