12 Choncho pa nthawi imeneyo tinatenga dzikoli kukhala lathu. Mafuko a Rubeni ndi Gadi+ ndinawapatsa Aroweli,+ mzinda umene uli m’chigwa cha Arinoni, ndi hafu ya dera lamapiri la Giliyadi, ndi mizinda yake.
9 Cholowa chawo chinayambira kumzinda wa Aroweli+ umene uli m’mphepete mwa chigwa cha Arinoni,+ ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho, kuphatikizapo malo onse okwererapo a Medeba+ mpaka kukafika ku Diboni.+