33 Fuko la Nafitali+ silinapitikitse anthu okhala m’mizinda ya Beti-semesi ndi Beti-anati,+ koma iwo anapitiriza kukhala pakati pa Akanani amene anali kukhala m’dzikolo.+ Ndipo fuko la Nafitali linayamba kugwiritsa ntchito yaukapolo anthu okhala m’mizinda ya Beti-semesi ndi Beti-anati.+