43 Aroni ndi ana ake azivala makabudula amenewa polowa m’chihema chokumanako kapena popita kuguwa lansembe kukatumikira pamalo oyera, kuti asapalamule mlandu ndi kufa. Limeneli ndi lamulo kwa iye ndi mbadwa zake mpaka kalekale.+
9 Ndiyeno Aroni ndi ana akewo uwamange malamba a pamimba. Ana akewo uwakulunge mipango kumutu kwawo ndipo unsembe udzakhala wawo. Limeneli ndi lamulo langa mpaka kalekale.+ Choncho upatse Aroni ndi ana ake mphamvu. +