27 Zimenezi zinachitikadi pamene Herode,* Pontiyo Pilato,+ pamodzi ndi anthu a mitundu ina komanso anthu a mu Isiraeli, anasonkhana mumzinda uno ndi kuukira Yesu, mtumiki wanu woyera,+ amene inu munamudzoza.+
38 Nkhani yake inali yonena za Yesu wa ku Nazareti, kuti Mulungu anamudzoza ndi mzimu woyera+ ndi mphamvu. Ndiponso kuti popeza Mulungu anali naye,+ anayendayenda m’dziko, n’kumachita zabwino ndi kuchiritsa onse osautsidwa ndi Mdyerekezi.+