26 M’mbali mwa khoma la pakhonde, m’zipinda zam’mbali za nyumbayo ndi pamzere wa matabwawo, munali mawindo a mafelemu aakulu mkati koma aang’ono kunja,+ ndipo anajambulamo zithunzi za mtengo wa kanjedza mbali zonse. Zithunzizi anazijambula mochita kugoba.