10 Achinyamata amene anakulira naye limodziwo anamuuza kuti: “Izi n’zimene mukanene+ kwa anthu awa amene akuuzani kuti, ‘Bambo anu anatisenzetsa goli lolemera, koma inuyo mutipeputsireko.’ Muwauze kuti, ‘Chala changa chaching’ono chidzakhala chachikulu kuposa chiuno cha bambo anga.+