31 Pambuyo pake Tera anatenga mwana wake Abulamu, mdzukulu wake+ Loti mwana wa Harana, Sarai+ mpongozi wake, mkazi wa mwana wake Abulamu, ndi kunyamuka kuchoka mumzinda wa Akasidi wa Uri, kupita kudziko la Kanani.+ Kenako, anafika ku Harana+ ndipo anakhala kumeneko.