Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 12:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ine ndidzadutsa m’dziko la Iguputo usiku umenewo+ ndi kupha mwana aliyense woyamba kubadwa m’dziko la Iguputo, mwana wa munthu kapena wa chiweto.+ Ndipo ndidzapereka ziweruzo pa milungu yonse ya mu Iguputo.+ Ine ndine Yehova.+

  • Yeremiya 43:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Nyumba za milungu ya Iguputo ndidzaziyatsa moto.+ Nebukadirezara adzatentha milunguyo ndi kuitenga kupita nayo kudziko lina. Monga mmene m’busa savutikira kuvala chovala chake,+ Nebukadirezara sadzavutika kugonjetsa dziko la Iguputo ndi kuchokako atapambana.

  • Yeremiya 46:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 “Yehova wa makamu, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Ine ndilanga Amoni+ wa ku No,+ Farao, Iguputo pamodzi ndi milungu yake+ ndi mafumu ake.+ Ndilanga Farao ndi onse amene amamukhulupirira.’+

  • Ezekieli 30:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 “Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Ndidzawononganso mafano onyansa+ ndi kuthetsa milungu yopanda pake ku Nofi.+ Sipadzapezekanso mtsogoleri wochokera m’dziko la Iguputo, ndipo ndidzachititsa anthu a m’dzikolo kukhala mwamantha.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena