32 “‘Chotero taonani! Masiku akubwera,’ watero Yehova, ‘pamene sadzatchulanso malowo kuti Tofeti ndiponso chigwa cha mwana wa Hinomu, koma adzawatchula kuti chigwa chopherako anthu.+ Iwo adzaika anthu m’manda ku Tofeti mpaka sikudzakhala malo okwanira.+