9 Ndidzawasandutsa chinthu chimene maufumu onse a padziko lapansi adzanthunthumira nacho, chifukwa cha masoka aakulu amene ndidzawagwetsera.+ Anthu a mitundu ina adzawatonza, kuwayesa chosereula, kuwanyoza+ ndipo adzakhala otembereredwa+ kulikonse kumene ndidzawabalalitsirako.+