5 Pa nthawi imeneyo, nkhope yako idzasangalala ukadzaona zimenezi.+ Mtima wako udzanthunthumira ndi kufutukuka, chifukwa chuma cha m’nyanja chidzabwera kwa iwe. Katundu wa mitundu ya anthu adzabwera kwa iwe.+
6 Inuyo mudzatchedwa ansembe a Yehova.+ Anthu adzakutchani atumiki+ a Mulungu wathu.+ Mudzadya zinthu zochokera ku mitundu ya anthu+ ndiponso mudzalankhula za inuyo mokondwera, chifukwa cha chuma ndi ulemerero zimene mudzapeze kwa mitunduyo.+