23 Iwo sadzadziipitsanso ndi mafano awo onyansa, zinthu zawo zonyansa ndi zochita zawo zonse zophwanya malamulo.+ Ndidzawapulumutsa ku machimo onse amene anali kuchita m’malo awo okhala, ndipo ndidzawayeretsa.+ Iwo adzakhala anthu anga ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo.+