6 Ine ndinali tcheru+ ndipo ndinali kuwamvetsera.+ Zimene iwo anali kunena sizinali zoona. Panalibe munthu wolapa zoipa zimene anachita,+ amene ananena kuti, ‘Kodi ndachitiranji zimenezi?’ Aliyense akubwerera kunjira imene anthu ambiri akuitsatira,+ ngati hatchi imene ikuthamangira kunkhondo.