-
Maliko 16:8Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
8 Tsopano iwo atatuluka, m’manda achikumbutsowo anayamba kuthawa, pakuti anali kunjenjemera ndi kunthunthumira kwambiri. Ndipo sanaulule kanthu kwa aliyense, chifukwa anagwidwa ndi mantha.+
MAWU OMALIZA AAFUPI
Mipukutu ndi Mabaibulo ena amene analembedwa pambuyo pake ali ndi mawu omaliza aafupi awa pambuyo pa Maliko 16:8:
Koma zinthu zonse zimene analamula, iwo anazifotokoza mwachidule kwa amene anali pafupi ndi Petulo. Komanso izi zitatha, Yesu mwiniyo anatumiza uthenga woyera ndi wosawonongeka wa chipulumutso chosatha kudzera mwa ophunzira, kuchokera kum’mawa mpaka kumadzulo.
-