18 “‘Mnaziriyo azimeta tsitsi+ la kumutu kwake, lomwe ndi chizindikiro cha unaziri wake. Azilimetera pakhomo la chihema chokumanako. Akatero, azitenga tsitsi la mutu wake wa unazirilo, n’kuliponya pamoto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
18 Koma Paulo atakhala kumeneko masiku ndithu, anatsanzikana ndi abalewo ndipo anapitiriza ulendo wake wa pamadzi kulowera ku Siriya. Pa ulendowu anatsagana ndi Purisikila ndi Akula. Paulo anameta tsitsi lake+ ku Kenkereya+ chifukwa cha lonjezo limene anachita.