Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 17:14, 15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Mukakalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani nʼkulitenga kukhala lanu ndipo mukukhalamo, ndiye inu nʼkunena kuti, ‘Tisankhe mfumu ngati mitundu ina yonse imene yatizungulira,’+ 15 mudzasankhe mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.+ Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Simukuloledwa kusankha mlendo amene si mʼbale wanu.

  • 1 Samueli 10:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Koma lero mwakana Mulungu wanu+ amene anakupulumutsani mʼmasautso anu onse ndiponso mʼmavuto anu, ndipo munanena kuti: “Ayi, mutisankhire mfumu yoti izitilamulira.” Tsopano imani pamaso pa Yehova potengera mafuko anu ndiponso mabanja anu.’”*

  • 1 Mbiri 1:43-50
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 43 Mafumu amene analamulira dziko la Edomu,+ Aisiraeli* asanayambe kulamulidwa ndi mfumu ina iliyonse,+ ndi awa: Bela mwana wa Beori. Dzina la mzinda wake linali Dinihaba. 44 Bela atamwalira, Yobabi mwana wa Zera wa ku Bozira,+ anayamba kulamulira mʼmalo mwake. 45 Yobabi atamwalira, Husamu wa ku Temani, anayamba kulamulira mʼmalo mwake. 46 Husamu atamwalira, Hadadi mwana wa Bedadi, amene anagonjetsa Amidiyani mʼdera la Mowabu, anayamba kulamulira mʼmalo mwake. Dzina la mzinda wake linali Aviti. 47 Hadadi atamwalira, Samila wa ku Masereka anayamba kulamulira mʼmalo mwake. 48 Samila atamwalira, Shauli wamumzinda wa Rehoboti, womwe unali mʼmbali mwa Mtsinje,* anayamba kulamulira mʼmalo mwake. 49 Shauli atamwalira, Baala-hanani mwana wa Akibori anayamba kulamulira mʼmalo mwake. 50 Baala-hanani atamwalira, Hadadi anayamba kulamulira mʼmalo mwake. Dzina la mzinda wake linali Pau ndipo mkazi wake dzina lake linali Mehetabele mwana wamkazi wa Matiredi, mwana wamkazi wa Mezahabu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena