Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 37:10-15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ndiyeno anapanga tebulo la mtengo wa mthethe+ masentimita 90 mulitali, masentimita 45 mulifupi ndi masentimita 70 kuchoka pansi mpaka mʼmwamba.+ 11 Analikuta ndi golide woyenga bwino ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira tebulo lonselo. 12 Analipangiranso felemu kuzungulira tebulo lonse muyezo wake masentimita 7* mulifupi mwake ndipo anapanga mkombero wagolide pafelemulo. 13 Kuwonjezera pamenepo, analipangira mphete 4 zagolide nʼkuziika mʼmakona ake 4 mmene munali miyendo yake 4. 14 Mphetezo zinali pafupi ndi felemu lija kuti muzilowa ndodo zonyamulira tebulolo. 15 Kenako anapanga ndodo zonyamulira za mtengo wa mthethe nʼkuzikuta ndi golide. Ndodo zimenezi zinali zonyamulira tebulolo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena