-
Numeri 4:14, 15Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
14 Aziikapo ziwiya zonse zimene amagwiritsa ntchito akamatumikira paguwa lansembe. Aziikapo zoikamo phulusa la zingwe za nyale, mafoloko aakulu, mafosholo, mbale zolowa ndi ziwiya zonse zapaguwa lansembe.+ Ndiyeno aziziphimba ndi zikopa za akatumbu, nʼkubwezeretsa mʼmalo mwake ndodo zake zonyamulira.+
15 Pamene mukusamutsa msasa, Aroni ndi ana ake azikhala atamaliza kuphimba zinthu za mʼmalo oyera+ ndi ziwiya zonse za mʼmalo oyerawo. Kenako ana a Kohati azibwera nʼkudzazinyamula+ koma iwo asamakhudze zinthu za mʼmalo oyerazo chifukwa akatero adzafa.+ Ana a Kohati ndi amene ali ndi udindo wonyamula zinthu zimenezi pachihema chokumanako.
-