-
Numeri 7:6-9Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
6 Choncho Mose analandira ngolo ndi ngʼombezo nʼkuzipereka kwa Alevi. 7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe 4 zamphongo kwa ana a Gerisoni, mogwirizana ndi zimene zinkafunika pa ntchito yawo.+ 8 Ana a Merari anawapatsa ngolo 4 ndi ngʼombe zamphongo 8, mogwirizana ndi zimene zinkafunika pa ntchito yawo imene ankagwira moyangʼaniridwa ndi Itamara, mwana wa wansembe Aroni.+ 9 Koma ana a Kohati sanawapatse zinthu zimenezi, chifukwa ntchito yawo inali yokhudza utumiki wapamalo oyera.+ Iwo ankanyamula zinthu zopatulika pamapewa awo.+
-