Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 28:1-3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 “Pakati pa Aisiraeli, usankhe Aroni+ mʼbale wako pamodzi ndi ana ake+ Nadabu, Abihu,+ Eleazara komanso Itamara+ kuti atumikire monga ansembe anga. 2 Aroni mʼbale wako umupangire zovala zopatulika kuti zimupatse ulemerero ndi kumʼkongoletsa.+ 3 Ulankhule ndi anthu onse aluso* amene ndinawapatsa mzimu wa nzeru.+ Anthuwo amupangire Aroni zovala zomwe zizisonyeza kuti wayeretsedwa, kuti atumikire monga wansembe wanga.

  • Ekisodo 28:40
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 40 Ana a Aroni uwapangirenso mikanjo, malamba ndi mipango* yokulunga kumutu+ kuti iwapatse ulemerero ndi kuwakongoletsa.+

  • Ekisodo 28:43
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 43 Aroni ndi ana ake azivala makabudula amenewa polowa mʼchihema chokumanako kapena popita kuguwa lansembe kukatumikira pamalo oyera kuti asapalamule mlandu nʼkufa. Limeneli ndi lamulo kwa iye ndi mbadwa* zake mpaka kalekale.”

  • Ekisodo 40:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Udzawadzoze ngati mmene unadzozera bambo awo+ kuti atumikire monga ansembe anga. Iwo akadzadzozedwa adzapitiriza kutumikira monga ansembe mʼmibadwo yawo yonse.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena