27 “Tsiku la 10 mʼmwezi wa 7 umenewu, ndi Tsiku la Mwambo Wophimba Machimo.+ Muzichita msonkhano wopatulika ndipo muzisonyeza kuti mukudzimvera chisoni*+ chifukwa cha machimo anu ndipo muzipereka nsembe yowotcha pamoto kwa Yehova.
7 Koma mʼchipinda chachiwiricho, mkulu wa ansembe yekha ndi amene ankalowamo kamodzi pa chaka,+ ndipo sankalowa popanda kutenga magazi.+ Magaziwo ankawapereka chifukwa cha iyeyo,+ komanso chifukwa cha machimo a anthu+ amene anawachita mosadziwa.