Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 32:35
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 35 Kubwezera ndi kwanga, chilangonso ndi changa.+

      Zimenezi zidzachitika pa nthawi yoikidwiratu phazi lawo likadzaterereka,+

      Chifukwa tsiku la tsoka lawo layandikira,

      Ndipo zowagwera zifika mofulumira.’

  • Yoswa 24:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Ndiyeno Yoswa anauza anthuwo kuti: “Simungathe kutumikira Yehova, chifukwa iye ndi Mulungu woyera.+ Iye ndi Mulungu amene amafuna kuti anthu azidzipereka kwa iye yekha.+ Sadzakhululuka zolakwa zanu* ndi machimo anu.+

  • Aroma 2:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Koma chifukwa chakuti sukufuna kusintha, ndipo ukusonyeza mtima wosalapa, Mulungu adzakulanga ndithu pa tsiku la mkwiyo wake akamadzaulula chiweruzo chake cholungama.+

  • 2 Petulo 2:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Ndipotu Mulungu sanalekerere angelo amene anachimwa aja+ osawapatsa chilango. Koma anawaponya mu Tatalasi,*+ anawamanga mumdima wandiweyani podikira kuti adzawaweruze.+

  • Yuda 14, 15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Ngakhalenso Inoki,+ wa mʼbadwo wa 7 kuchokera kwa Adamu, analosera za iwowa pamene anati: “Taonani! Yehova* anabwera ndi angelo ake masauzandemasauzande+ 15 kudzaweruza anthu onse,+ ndi kudzagamula kuti onse osaopa Mulungu apezeka ndi mlandu chifukwa cha zinthu zonyoza Mulungu zimene anachita, komanso chifukwa cha zinthu zonse zoipa kwambiri zimene ochimwa osaopa Mulunguwa anamunenera.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena