13 Koma ngati munthu si wodetsedwa kapena sanali pa ulendo, ndipo wanyalanyaza kukonza nsembe ya Pasika, munthuyo aziphedwa kuti asakhalenso pakati pa anthu ake,+ chifukwa sanapereke nsembeyo kwa Yehova pa nthawi imene inaikidwiratu. Munthuyo adzafa chifukwa cha tchimo lake.