Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Numeri 22:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Choncho akuluakulu a ku Mowabu ndi a ku Midiyani anapita kwa Balamu+ atatenga ndalama zoti akamulipire kuti awawombezere maula, komanso anamuuza zimene Balaki ananena.

  • Numeri 25:1-3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Pa nthawi imene Aisiraeli ankakhala ku Sitimu,+ anayamba kuchita chiwerewere ndi akazi a ku Mowabu.+ 2 Akaziwo anaitana Aisiraeliwo kuti azikapereka nsembe kwa milungu yawo+ ndipo Aisiraeliwo anayamba kudya nsembezo komanso kugwadira milungu ya Amowabu.+ 3 Choncho Aisiraeli anayamba kulambira nawo Baala wa ku Peori,+ ndipo Yehova anakwiya kwambiri ndi Aisiraeliwo.

  • Numeri 25:17, 18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 “Akhaulitseni Amidiyani ndipo muwaphe,+ 18 chifukwa akubweretserani tsoka mochenjera pokukopani kuti muchimwe ku Peori.+ Muwaphe ndithu, chifukwanso cha zochita za mchemwali wawo Kozibi, mwana wa mtsogoleri wa ku Midiyani, amene anaphedwa+ pa tsiku limene mliri unakugwerani chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”+

  • 1 Akorinto 10:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Komanso tisamachite chiwerewere,* mmene ena a iwo anachitira, nʼkufa anthu 23,000 tsiku limodzi.+

  • Chivumbulutso 2:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Ngakhale zili choncho, ndakupeza ndi milandu ingapo. Iwe kumeneko uli ndi anthu amene akupitiriza kutsatira chiphunzitso cha Balamu,+ amene anaphunzitsa Balaki+ kuti aikire ana a Isiraeli chopunthwitsa kuti adye zoperekedwa nsembe kwa mafano ndi kuchita chiwerewere.*+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena