-
Numeri 23:13, 14Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
13 Balaki anauza Balamu kuti: “Tiyeni tipite kumalo ena kumene mungathe kuwaona anthuwo. Simukaona onse, koma mukangoona ochepa. Mukatemberere amenewo.”+ 14 Choncho anamutengera ku Zofimu, pamwamba pa phiri la Pisiga.+ Kumeneko anamanga maguwa ansembe 7, nʼkupereka nsembe ngʼombe yamphongo ndi nkhosa yamphongo paguwa lililonse.+
-