-
Numeri 21:23, 24Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
23 Koma Sihoni sanalole kuti Aisiraeli adutse mʼdziko lake. Mʼmalomwake, iye anasonkhanitsa anthu ake onse nʼkupita kukamenyana ndi Aisiraeli mʼchipululumo. Anakafika ku Yahazi ndipo anayamba kumenyana ndi Aisiraeli.+ 24 Koma Aisiraeli anapha anthuwo ndi lupanga+ nʼkuwalanda dziko lawo,+ kuyambira kuchigwa cha Arinoni+ mpaka kuchigwa cha Yaboki,+ pafupi ndi Aamoni, chifukwa Yazeri+ anachita malire ndi Aamoni.+
-
-
Numeri 21:33-35Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
33 Pambuyo pake, anatembenuka nʼkulowera Njira ya ku Basana. Ndiyeno Ogi+ mfumu ya ku Basana anabwera limodzi ndi anthu ake onse kudzamenyana nawo ku Edirei.+ 34 Yehova anauza Mose kuti: “Usamuope ameneyu,+ chifukwa ndipereka iyeyo pamodzi ndi anthu ake onse komanso dziko lake mʼmanja mwako+ ndipo umuchitire zimene unachitira Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankakhala ku Hesiboni.”+ 35 Choncho Aisiraeliwo anapha iyeyo, ana ake ndi anthu ake onse, moti palibe ndi mmodzi yemwe amene anapulumuka,+ ndipo analanda dziko lake.+
-