-
Nehemiya 10:28-30Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
28 Anthu ena onse, ansembe, Alevi, alonda apageti, oimba, atumiki apakachisi* ndiponso aliyense amene anadzipatula kwa anthu amʼmayikowo kuti asunge Chilamulo cha Mulungu woona,+ akazi awo, ana awo aamuna ndi aakazi ndiponso aliyense wodziwa zinthu komanso woti akhoza kumvetsa zimene zikunenedwa, 29 anagwirizana ndi abale awo, anthu otchuka. Iwo analumbira* kuti azitsatira Chilamulo cha Mulungu woona chimene chinaperekedwa kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu woona komanso kuti azitsatira mosamala malamulo onse, ziweruzo ndi mfundo za Yehova Ambuye wathu. 30 Komanso kuti sitidzapereka ana athu aakazi kwa anthu amʼdzikoli ndiponso sitidzatenga ana awo aakazi nʼkuwapereka kwa ana athu aamuna.+
-