Mateyu 22:43, 44 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 43 Iye anawafunsanso kuti: “Nanga nʼchifukwa chiyani mouziridwa ndi mzimu,+ Davide anamutchula kuti Ambuye, pamene ananena kuti, 44 ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditaika adani ako pansi pa mapazi ako”’?+ Maliko 12:36 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 36 Kudzera mwa mzimu woyera,+ Davideyo ananena kuti, ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditaika adani ako pansi pa mapazi ako.”’+ Luka 20:42, 43 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 42 Chifukwa Davideyo ananena mʼbuku la Masalimo kuti, ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja 43 mpaka nditaika adani ako kuti akhale chopondapo mapazi ako.”’+ Machitidwe 2:34, 35 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 34 Ndipotu Davide sanapite kumwamba, koma iyeyo anati, ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja 35 mpaka nditaika adani ako kuti akhale chopondapo mapazi ako.”’+ 1 Akorinto 15:25 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 25 Chifukwa ayenera kukhala mfumu nʼkumalamulira mpaka Mulungu ataika adani onse pansi pa mapazi ake.+ Aheberi 1:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Iye amasonyeza bwino ulemerero wa Mulungu+ ndipo ndi chithunzi chenicheni cha Mulunguyo.+ Komanso mawu ake amphamvu amathandiza kuti zinthu zikhalepobe. Ndipo atatiyeretsa potichotsera machimo athu,+ anakhala kudzanja lamanja la Wolemekezeka kumwamba.+ Aheberi 1:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Koma kodi ndi mngelo uti amene anamuuzapo kuti: “Khala kudzanja langa lamanja, mpaka nditaika adani ako kuti akhale chopondapo mapazi ako”?+ Aheberi 10:12, 13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 12 Koma munthu ameneyu anapereka nsembe imodzi yamachimo yothandiza mpaka kalekale, ndipo anakhala kudzanja lamanja la Mulungu.+ 13 Kuyambira nthawi imeneyo, akudikira mpaka pamene adani ake adzaikidwe kuti akhale chopondapo mapazi ake.+
43 Iye anawafunsanso kuti: “Nanga nʼchifukwa chiyani mouziridwa ndi mzimu,+ Davide anamutchula kuti Ambuye, pamene ananena kuti, 44 ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditaika adani ako pansi pa mapazi ako”’?+
36 Kudzera mwa mzimu woyera,+ Davideyo ananena kuti, ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditaika adani ako pansi pa mapazi ako.”’+
42 Chifukwa Davideyo ananena mʼbuku la Masalimo kuti, ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja 43 mpaka nditaika adani ako kuti akhale chopondapo mapazi ako.”’+
34 Ndipotu Davide sanapite kumwamba, koma iyeyo anati, ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja 35 mpaka nditaika adani ako kuti akhale chopondapo mapazi ako.”’+
25 Chifukwa ayenera kukhala mfumu nʼkumalamulira mpaka Mulungu ataika adani onse pansi pa mapazi ake.+
3 Iye amasonyeza bwino ulemerero wa Mulungu+ ndipo ndi chithunzi chenicheni cha Mulunguyo.+ Komanso mawu ake amphamvu amathandiza kuti zinthu zikhalepobe. Ndipo atatiyeretsa potichotsera machimo athu,+ anakhala kudzanja lamanja la Wolemekezeka kumwamba.+
13 Koma kodi ndi mngelo uti amene anamuuzapo kuti: “Khala kudzanja langa lamanja, mpaka nditaika adani ako kuti akhale chopondapo mapazi ako”?+
12 Koma munthu ameneyu anapereka nsembe imodzi yamachimo yothandiza mpaka kalekale, ndipo anakhala kudzanja lamanja la Mulungu.+ 13 Kuyambira nthawi imeneyo, akudikira mpaka pamene adani ake adzaikidwe kuti akhale chopondapo mapazi ake.+