110 Yehova anauza Ambuye wanga kuti:
“Khala kudzanja langa lamanja+
Mpaka nditaika adani ako kuti akhale chopondapo mapazi ako.”+
2 Yehova adzatambasula ndodo yako yachifumu kuti ulamulirenso madera ena osati mu Ziyoni mokha. Iye adzanena kuti:
“Pita pakati pa adani ako ndipo ukawagonjetse.”+