Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 14:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Ndipo Melekizedeki,+ mfumu ya mzinda wa Salemu,+ anabweretsa mkate ndi vinyo. Iyeyu anali wansembe wa Mulungu Wamʼmwambamwamba.+

  • Aheberi 5:5, 6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Zilinso chimodzimodzi ndi Khristu. Iye sanadzipatse yekha ulemerero+ podziika yekha kukhala mkulu wa ansembe. Koma amene anamupatsa ulemerero umenewo ndi amene anamuuza kuti: “Iwe ndiwe mwana wanga. Lero ine ndakhala bambo ako.”+ 6 Ngatinso mmene akunenera penapake kuti: “Iwe ndiwe wansembe mpaka kalekale, mofanana ndi unsembe wa Melekizedeki.”+

  • Aheberi 6:19, 20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Chiyembekezo chathuchi+ chili ngati nangula* wa miyoyo yathu ndipo nʼchotsimikizika komanso chokhazikika. Chiyembekezochi chimatilowetsa mkati, kuseri kwa katani yotchingira+ 20 kumene Yesu, yemwe ndi kalambulabwalo, anakalowa chifukwa cha ife.+ Iyeyu ndi mkulu wa ansembe mpaka kalekale mofanana ndi unsembe wa Melekizedeki.+

  • Aheberi 7:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Popeza analibe bambo, analibe mayi, analibe mzere wa makolo ndipo tsiku limene anabadwa komanso limene anamwalira silikudziwika, koma anamuchititsa kuti afanane ndi Mwana wa Mulungu, iye ndi wansembe mpaka kalekale.+

  • Aheberi 7:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Kukhala ndi ansembe a fuko la Levi kunali mbali ya Chilamulo cha Mose chimene Aisiraeli anapatsidwa. Ndiye zikanakhala kuti ansembe a fuko la Levi angathandize anthu kukhala angwiro,+ kodi pakanafunikanso wansembe ngati Melekizedeki?+ Kodi sizikanakhala zokwanira kungokhala ndi wansembe ngati Aroni?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena